Cholinga cha lamuloli ndi chikondi/The aim of the charge is love

09/04/2024 30 min

Listen "Cholinga cha lamuloli ndi chikondi/The aim of the charge is love"

Episode Synopsis

1 Timoteyo 1:5-7 m’mavesi amenewa, Paulo mtumwi akuonetsera kufunika kolalikira mawu a mulungu kwa anthu. Iye akunena kuti ndi lamulo lochokera kwa olamulira wamkulu limene limaperekedwa kwa abusa onse omwe ali mchoonadi. Yesu monga iye mwini ulamuliro, akulamulira abusa onse kuti alalikire mawu a mulungu mpaka kumalekezero adziko lapansi kenako mathero azafika. M’busa kuti alalikire, akuyenera kukhala ndi chikondi pa anthu omwe akuwalalikira komanso amve kusoweka komwe anthu alinako kofunikira chipulumutso. Nchifukwa chake tinganene kuti cholinga cha lamuloli ndi chikondi monga momwe Paulo mtumwi akuyankhulira.
 
1 Timothy 1:5-7 in these verses, the apostle Paul puts emphasis on the need to preach the word of God to people. He says that it is a charge that all true pastors receive from higher authority. Jesus as the one with authority, he charges all pastors to preach the word of God to the ends of the earth and then the end will come. But for a true pastor to preach, he must have deep love for God’s people and feel the need to rescue them all through the preaching of the gospel. Therefore, we can conclude to say that the aim of the charge is love as the apostle Paul puts it.